Alipire chindapusa cha K5.5 million Kaamba koluma ndi kudula phuno ya membala wa MCP

0
281

Bwalo la milandu la Kasungu lalamula m’modzi mwa otsogolera achinyamata ku chipani cha UTM mchigawo chapakati, a Alick Saini kuti apereke K5,050,000 ngati chindapusa kaamba koluma ndikudula mphuno ya Chisomo Kefa, mtsogoleri wa achinyama a MCP.

A Saini adapalamula mlanduwu pa 1 September chaka chino atasemphana chichewa ndi a Kefa pa nkhani za pa chiweniweni.

Mwa ndalamazi K4.5 miliyoni ndi chipukuta misonzi chopitsa kwa Kefa pomwe K550,000 ndi yopita ku boma.

Asaini akuyenera kupereka K1.5 miliyoni kwa a Kefa komanso K550,000 ku boma lero kuti awamasule ndipo ndalama yotsalayo awapatsa miyezi isanu kuti amalize.

Magistrate Jones Masula wabwaloli wati wapereka chilangochi chifukwa zomwe adachita a Saini zidapereka chilema chamuyaya kwa a Kefa.

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here